top of page
Search

BUNGWE LA ATUMIKI ACHIFUNDO LIYAMBA NTCHITO YAKE POFIKIRA A SISTERI A POOR CLARE

Updated: Nov 1

ree

Bungwe la Atumiki a Chifundo kuchokera pa parishi ya Maula lati lili ndi chiyembekezo choti likwanitsa kufikira anthu ochuluka ndi ntchito zake za chifundo mu chaka chino cha 2024.


Wayankhula izi ndi wapampando wabungweli, mayi Artemisia Windo pambuyo pochita ntchito zachifundo kwa ma sisteri obindikira a Poor Clare ku Maula lero pa 09 March 2024.


Amayi Windo ati anachiwona chinthu chofunika kwambiri kuyamba utumiki wawo wogwira ntchito za chifundo mu chaka chino poyendera ma sisteriwa.


" Ife ngati Atumiki a Chifundo apa Maula tinachiona cha nzeru kuti 2024, utumiki wathu tiyambire kwa masisteri athu a kwa Poor Clare omwe timakhala nawo pompano. Amati 'Charity begins at home'," anatero Mayi Windo.


Bungwe la Atumiki Achifundo la pa parishi ya Maula lakhala likugwira ntchito za chifundo zosiyanasiyana monga kuyendera odwala m'zipatala, kuyendera ansembe komanso anthu achikulire.


Wolemba ndi Bro. Julius Collen Chalunda

 
 
 

Comments


ABOUT US

We are simply known as a Cathedral of Lilongwe, which is the Capital City of Malawi. We belong to the metropolitan Archdiocese of Lilongwe whose safragan dioceses are Dedza, Mzuzu and Karonga. We follow the Roman or Latin rite.

ADDRESS

+265 (0) 1 755 846

+265 (0) 998 73 35 93

P.O Box 1524, Lilongwe.

info@maulaparish.org

louis2chikanya@gmail.com

SUBSCRIBE FOR EMAILS

Thanks for submitting!

  • Facebook
  • Instagram
  • Twitter

© 2025 by Team iWork. Proudly created with Wix.com

bottom of page