top of page
Search

CHAKA CHA EPIFANIA KU MAULA PARISHI


Bambo mfumu a parishi ya Maula, bambo Francis Lekaleka alimbikitsa ana a Tilitonse pa parishiyi kukhala okonda kupemphera komanso ophathana ndi mulungu nthawi zonse


Bambo Lekaleka alankhula izi Lamulungu pa mwambo wa nsembe ya Ukalistiya ya Epifaniya pa parishiyi.


Bambo Lekaleka kuwerenga uthenga wabwino


Apa Iwo ati Epifaniya ya chaka chino ithandizire kusintha miyoyo ya anawa pomweso pano alowa chaka chatsopano.


Bambo Lekaleka akumbutsaso makolo kuti alimbikitse anawa kukonda moyo wopemphera ndi cholinga chofuna kuwathandizira kuyenda m'moyo wa chikhristu nthawi zonse ndi kutenga chitsanzo chabwino cha Maria ndi Yosefe cholimbikitsa anawa kuti adziphathana ndi Yesu Khristu nthawi zonse.


Mwazina, Iwo ati akulingalira zokonza njira zoti anawa adzitenga nawo gawo m'zochitika zosiyanasiyana monga kupembedza ambuye Yesu okhala mu Ukalistiya komanso kutsogolera mapemphero a Kolona.


Liwu lakuti Epifaniya limachokera ku Chigiriki ndipo limatanthauza kuti kuonekera kwa Mulungu pakati pa anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi.


Nyengoyi imakumbukiranso kubwera kwa anzeru aku m'mawa amene amatchedwanso Akatswiri a Nyenyezi aku Mmawa (The Magi).


 
 
 

Comments


ABOUT US

We are simply known as a Cathedral of Lilongwe, which is the Capital City of Malawi. We belong to the metropolitan Archdiocese of Lilongwe whose safragan dioceses are Dedza, Mzuzu and Karonga. We follow the Roman or Latin rite.

ADDRESS

+265 (0) 1 755 846

+265 (0) 998 73 35 93

P.O Box 1524, Lilongwe.

info@maulaparish.org

louis2chikanya@gmail.com

SUBSCRIBE FOR EMAILS

Thanks for submitting!

  • Facebook
  • Instagram
  • Twitter

© 2025 by Team iWork. Proudly created with Wix.com

bottom of page