top of page
Search

La Mulungu La Chifundo cha Mulungu ku Maula Cathedral

Bungwe la Chifundo cha Mulungu pa parishi ya Maula lachita nawo chaka cha la Mulungu la Chifundo cha Mulungu lero pa 12 April 2026.


Mwambo wa nsembe ya chakachi unatsogoleredwa ndi bambo Peter Makina.


Mu ulariki wawo, bambo Makina anapempha akhristu kukhala okonda kuthandizana nthawi zonse kuphatikizapo pa mavuto osiyanasiyana ndipo kuti adzichita izi ndi chikhulupiliro.


Bambo Makina kutsogolera mwambo wa nsembe ya Misa ya Lamulungu la Chifundo cha Mulungu
Bambo Makina kutsogolera mwambo wa nsembe ya Misa ya Lamulungu la Chifundo cha Mulungu

"Tiyeni akhristu tithandiza anzathu. Kodi Ife timachita zotani? Kodi ine ndimamvera chifundo anzanga? Tiyeni tichitire chifundo azathu kuti nawonso akachitire chifundo ena" anatero bambo Makina.


Iwo apemphanso akhristuwa kuleka kukhala okaika ndikukhala anthu okhupilira nthawi zonse. Bambo Makina ati akhristu "tikamalandira Ukaristia tidziti 'ndikukhulupiliradi ambuye Yesu okhala mu Ukaristia.'



Ndipo pomaliza, iwo apempha akhristu kuthandiza anthu omwe ndi osowa kuphatikizapo omwe amapempha minsewu posatengera mphulupulu zawo,


"Amene akuvutika aja tiwathandize posatengera zochita zawo, monga ana a m'misewu tisatengere kuti amaba koma tiwathandize ndipo tisatope kuchita zabwino," anamaliza motero bambo Makina

 
 
 

Comments


ABOUT US

We are simply known as a Cathedral of Lilongwe, which is the Capital City of Malawi. We belong to the metropolitan Archdiocese of Lilongwe whose safragan dioceses are Dedza, Mzuzu and Karonga. We follow the Roman or Latin rite.

ADDRESS

+265 (0) 1 755 846

+265 (0) 998 73 35 93

P.O Box 1524, Lilongwe.

parishpriest@maulaparish.org

administration@maulaparish.org

SUBSCRIBE FOR EMAILS

Thanks for submitting!

  • Facebook
  • Instagram
  • Twitter

© 2025 by Team iWork. Proudly created with Wix.com

bottom of page