top of page
Search

"Ukaristiya Thupi ndi Magazi a Ambuye yesu"

Akhristu kuchokera pa parishi ya Maula alangizidwa kukhala anthu okonda kulandira Ukaristia nthawi zonse.


Bambo Peter Makina ndi omwe alankhula izi kudzera mu ulaliki wawo pa mwambo wa nsembe ya Misa ya Chaka Cha Ukaristia.


Bambo Makina anati akhristu akalandira thupi la Ambuye Yesu moyo wawo udzisinthika popeza "Ukaristia azifanafana ndi Yesu mwini popeza munthu aliyense amakhala chomwe amadya."


Ndipo iwo anaonjezera kuti akhristu asanalandire ukaristia, akuyenera kuyamba kukonza mu mtima mwawo polandira sakamenti la kulapa, kuti ambuye apeze mtima muli bwino.


Bambo Makina anapitilira kupempha akhristu kuti adzipita nthawi yabwino ku mwambo wa nsembe ya Ukaristiya chifukwa anthu ena amapita mwachangu ku misokhano ya ndale angakhalenso ku mpira, pomwe ku tchalitchi timachedwa.


Pomaliza, iwo anatsindika kuti Ukaristia umalimbikitsa moyo wa chikhristu chifukwa ndi chakudya cha uzimu.







 
 
 

Comments


ABOUT US

We are simply known as a Cathedral of Lilongwe, which is the Capital City of Malawi. We belong to the metropolitan Archdiocese of Lilongwe whose safragan dioceses are Dedza, Mzuzu and Karonga. We follow the Roman or Latin rite.

ADDRESS

+265 (0) 1 755 846

+265 (0) 998 73 35 93

P.O Box 1524, Lilongwe.

parishpriest@maulaparish.org

administration@maulaparish.org

SUBSCRIBE FOR EMAILS

Thanks for submitting!

  • Facebook
  • Instagram
  • Twitter

© 2025 by Team iWork. Proudly created with Wix.com

bottom of page