Abambo a Bungwe la CMA Alimbikitsidwa Kuiika Chikhulupiriro Patsogolo M'malo mwa "Nthawi Zotanganidwa"
- Communications
- Jan 31
- 1 min read

Bungwe la abambo la CMA la pa parishi ya Maula lapemphedwa kukhala lochilimika potumikira Mulungu komanso kupezeka kwa ma membala ake pa mikumano yomwe limakhala nayo.
Pempholi laperekedwa ndi wapampando wa bungweli, a Steve Chipala pambuyo pa mwambo wa nsembe ya Misa yotolera limodzi limodzi womwe unachititsidwa ndi bungwe la abambo, mu Arkidayosizi ya Lilongwe ku parishi ya St. Kizito, Chigoneka.
Mwambo wansembe ya Misayi unatsogoleredwa ndi Episkopi mthandizi wa Arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa omwe analimbikitsa abambowa kumakhala patsogolo ndikuganizirapo za udindo wawo potukula mpingo pomwenso dziko lino likhale likukondwelera zaka 125 zakupezeka kwa mpingo wachiKatolika kuno ku Malawi chaka chino.

A Chipala ati uthenga wa ambuye Mwakhwawa wa lero uthandizire kusintha abambo ambiri kuti asunthire chifupi ndi Mulungu pofuna kumanga mpingo wamphamvu.
Iwo ati zimakhala zokhumudwitsa nthawi zambiri kuona abambo ambiri asakutenga nawo mbali muzochitika za mu mpingo ponena kuti amakhala otanganidwa.
"Tiyeni a zibambo anzanga tichilimike potenga nawo gawo mu zochitika za mu mpingo pofuna kumanga mpingo wa mtsogolo," anatero a Chipala.
Bungwe la abamboli lachita mwambowu ndicholinga chofuna kupeza ndalama za msonkhano wa bungweli mdziko muno wapachaka womwe udzachitikire mu Arkidzayosiziyi mwezi wa March.
Wolemba ndi Peter Dumayo



Comments