Lamulungu La Mayitanidwe ku Parishi ya Maula m'chaka cha 2026
- Edwin Sitima
- Apr 29
- 1 min read
Achinyamata awapempha kumvetsera ndi kuyankha mayitanidwe awo moyenera omwe Mulungu akuwayitanira.
Bambo Peter Makina ndi omwe ayankhula izi pa mwambo wa nsembe ya Ukaristiya ya chaka cha mayitanidwe, ku Maula Cathedral mu Arkidayosizi ya Lilongwe.

Bambo Makina anati makolo ali ndi ntchito yambiri yothandiza ndi kulimbikitsa achinyamata kut ayankhe mayitanidwe oyenera, monga moyo wa unsembe, ubulazala, uSisteri komaso moyo wa m'banja, komaso moyo okhala pa yekha.
"Makolo tiyeni tikhale abusa abwino, polimbikitsa ana kutumikira Mulungu mwa njira yosiyanasiyana, m'busa wabwino amamva fungo la nkhosa zake."
Mpingo waKatolika pa dziko lonse lamulungu lachinayi mu nyengo ya Pasaka umakumbutsa achinyamata kuti amve mayitanidwe otumikira Mulungu potsatira mapazi a yesu Khristu yemwe ndi m'busa wabwino.
Pa Mwambo wa nsembe ya Ukaristiya, kwaya ya Bunda Catholic Alumni, ndiyomwe inatsogolera maimbidwe ndipo wapampando wa chipembezo pa parish ya Maula anathokoza kwayayi kamba ka utumiki wake.













Comments