Utumiki wa abambo pa parishi ya Maula upitilira kulimbikitsidwa
- Edwin Sitima
- May 3
- 1 min read
Nthawi ndi nthawi mabungwe komanso miphakati imene ili pansi pa parish ya Maula mu Arkidayosizi ya Lilongwe imatenga nawo gawo pa kutsogolera chipembedzo.
Limodzi mwa mabungwe lomwe layendetsa kale chipembedzo ndi bungwe la a bambo a chiKatolika la CMA ndipo parishi ya Maulayi yathokoza bungweli kamba kodzipereka kwake potsogolera chipembedzo.

Mwazina, abambowo, Loweruka pa 2 May 2026, anakoza mu tchalitchi cha Maula komanso kusamala malo ena pa parishiyi.
Ndipo iwo sanalekere pomwepo ayi, tsiku la Mulungu pa 3 May 2026, anaperekera mphatso za paguwa komaso kuwerenga mau.
Chakumadzulo, abambowa anakumana pamodzi kunyumba ya ansembe a pa parishiyi, pofuna kucheza ngati banja limodzi la pa Maula Cathedral Parishi.














Comments