ATSOGOLERI A BUNGWE LA CWA AKUMANA NDI BAMBO MFUMU
- Edwin Sitima
- Feb 22
- 1 min read

Atsogoleri a bungwe la amayi a chiKatolika la CWA, pa parishi ya Maula anakumana ndi bambo mfumu a parishiyi, Bambo Francis Lekalek, lamulungu pa 22 February 2026 ndi cholinga chofuna kuwadziwitsa za atsogoleriwa komanso kudziwa ntchito zimene bungweli limagwira, zovuta zimene bungweli limakumana nazo komanso mmene bungweli limagwira ntchito ndi ma bungwe ena.
Adindowa anafotokozerapo zambiri za bungweli monga kusonkha ndalama zofunika kuyendetsa bungweli, kuyendetsa chipembedzo, kutumikira ntchito za chifundo komanso kulumikizana bwino ndi dinale ya Maula.
Amayiwa anafotokonzeraponso za kuchepa kwa a mayi omwe amabwera ku misonkhano ya pa mwezi komanso kukakhala zochitika za parishi.
M'mawu awo, bambo Lekaleka anati mikumano ya amayi ndi yofunika kwambiri kuti bungweli lidziyenda bwino.
Iwo analangizanso amaiwa kuti achilimike pa njira za uzimu wao maka popanga mibindikiro ndikuwalangiza kuti apange mwachangu mlozo wa chaka chino cha 2026 kuti zonse ziziyenda mu ndondomeko yake.



Comments